Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:31-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo kudangotero kuti wansembe wina anatsika njirayo, ndipo pakumuona iye anapita mbali yina.

32. Momwemonso Mlevi, pofika pamenepo, ndi kumuona, anapita mbali yina.

33. Koma Msamariya wina ali pa ulendo wace anadzapali iye; ndipo pakumuona, anagwidwa cifundo,

34. nadza kwa iye, namanga mabala ace, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yace ya iye yekha, nadza naye ku nyumba ya alendo, namsungira.

35. Ndipo m'mawa mwace anaturutsa marupiya atheka awiri napatsa mwini nyumba ya alendo, nati, Msungire iye, ndipo ciri conse umpatsa koposa, ine, pobwera, ndidzakubwezera iwe.

36. Uti wa awa atatu, uyesa iwe, anakhala mnansi wa iye uja adagwa m'manja a acifwamba?

Werengani mutu wathunthu Luka 10