76. 19 Eya, ndipo iwetu kamwanawe, udzanenedwa mneneri wa Wamkulukulu:20 Pakuti udzatsogolera Ambuye, kukonza njira zace;
77. Kuwapatsa anthu ace adziwitse cipulumutso,21 Ndi makhululukidwe a macimoao,
78. Cifukwa ca mtima wacifundo wa Mulungu wathu.M'menemo mbanda kuca wa kumwamba udzaticezera ife;
79. 22 Kuwalitsira iwo okhala mumdima ndi mthunzi wa imfa;Kulunjikitsa mapazi athu mu njira ya mtendere.
80. Ndipo mwanayo anakula, nalimbika mu mzimu wace, ndipo 23 iye anali m'mapululu, kufikira masiku akudzionetsa yekha kwa Israyeli.