Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:58-69 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

58. Ndipo anansi ace ndi abale ace anamva kuti Ambuye anakulitsa cifundo cace pa iye; 9 nakondwera naye pamodzi.

59. Ndipo panali 10 tsiku lacisanu ndi citatu iwo anadza kudzadula kamwanako; ndipo akati amuche dzina la atate wace Zakariya.

60. Ndipo amace anayankha, kuti, lai; koma 11 adzachedwa Yohane.

61. Ndipo iwo anati kwa iye, Palibe wina wa abale ako amene achedwa dzina ili.

62. Ndipo anakodola atate wace, afuna amuche dzina liti?

63. Ndipo iye anafunsa colemberapo, nalemba, kuti, Dzina lace ndi Yohane. Ndipo anazizwa onse.

64. Ndipo 12 pomwepo panatseguka pakamwa pace, ndi lilume lace linamasuka, ndipo iye analankhula, nalemekeza Mulungu.

65. Ndipo panagwa mantha pa iwo onse akukhala oyandikana nao; ndipo analankhulalankhula nkhani izi zonse m'dziko: lonse la mapiri a Yudeya,

66. Ndipo onse amene anazimva anazisunga m'mtima mwao, nanena, Nangamwana uyu adzakhala wotani? Pakuti 13 dzanja la Ambuye linakhala pamodzi ndi iye.

67. Ndipo atate wace Zakariya anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nanenera za Mulungu, nati,

68. Wolemekezeka Ambuye, Mulungu wa Israyeli;14 Cifukwa iye anayang'ana, nacitira anthu ace ciombolo,

69. Ndipo iye anatikwezera ife nyanga ya cipulumutso,Mwa pfuko la Davine mwana wace,

Werengani mutu wathunthu Luka 1