Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:52-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

52. iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu,Ndipo anakweza aumphawi,

53. 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino,Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.

54. Anathangatira Israyeli mnyamata wace,Kuti akakumbukile cifundo,

55. 8 (Monga analankhula kwa makolo athu)Kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yace ku nthawi yonse.

56. Ndipo Mariya anakhala ndi iye ngati miyezi itatu, nabweranso kunyumba kwace.

57. Ndipo inakwanira nthawi ya Elisabeti, ya kubala kwace, ndipo anabala mwana wamwamuna.

58. Ndipo anansi ace ndi abale ace anamva kuti Ambuye anakulitsa cifundo cace pa iye; 9 nakondwera naye pamodzi.

Werengani mutu wathunthu Luka 1