Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:44-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Pakuti ona, pamene mau a kulankhula kwako analowa m'makutu anga, mwana anatsalima ndi msangalalo m'mimba mwanga.

45. Ndipo wodala ali iye amene anakhulupirira; cifukwa zidzacitidwa zinthu zimene Ambuye analankhula naye.

46. 3 Ndipo Mariya anati,Moyo wanga ulemekeza Ambuye,

47. Ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

48. Cifukwa iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wace;Pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzandichula ine wodala.

49. Cifukwa iye Wamphamvuyo anandicitira ine zazikuru;4 Ndipo dzina lace liri loyera.

50. 5 Ndipo cifundo cace cifikira anthu a mibadwo mibadwoPa iwo amene amuopa iye.

51. Iye anacita zamphamvu ndi mkono wace;6 Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao,

52. iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu,Ndipo anakweza aumphawi,

53. 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino,Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.

54. Anathangatira Israyeli mnyamata wace,Kuti akakumbukile cifundo,

55. 8 (Monga analankhula kwa makolo athu)Kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yace ku nthawi yonse.

56. Ndipo Mariya anakhala ndi iye ngati miyezi itatu, nabweranso kunyumba kwace.

57. Ndipo inakwanira nthawi ya Elisabeti, ya kubala kwace, ndipo anabala mwana wamwamuna.

Werengani mutu wathunthu Luka 1