Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:25-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ambuye wandicitira cotero m'masiku omwe iye anandipenyera, kucotsa manyazi anga pakati pa anthu.

26. Ndipo mwezi wacisanu ndi cimodzi mngelo Gabrieli anatumidwa ndi Mulungu kunka ku mudzi wa ku Galileya dzina lace N azarete,

27. kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, dzina lace Yosefe, wa pfuko la Davine; ndipo dzina lace la namwaliyo ndilo Mariya.

28. Ndipo pakulowa mngelo anati kwa iye, Tikuoneni, wocitidwa cisomo, Ambuye ali ndi iwe.

29. Koma iye ananthunthumira ndi mau awa, nasinkhasinkha kulankhula uku nkutani.

30. Ndipo mngelo anati kwa iye, Usaope, Mariya; pakuti wapeza cisomo ndi Mulungu.

31. Ndipo taona, udzakhala ndi pakati, nudzabala mwana wamwamuna, nudzamucha dzina lace Yesu.

Werengani mutu wathunthu Luka 1