Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo kunali, pamene masiku a utumiki wace anamarizidwa, anamuka kunyumba kwace.

24. Ndipo atatha masiku awa, Elisabeti mkazi wace anaima; nadzibisa miyezi isanu, nati,

25. Ambuye wandicitira cotero m'masiku omwe iye anandipenyera, kucotsa manyazi anga pakati pa anthu.

26. Ndipo mwezi wacisanu ndi cimodzi mngelo Gabrieli anatumidwa ndi Mulungu kunka ku mudzi wa ku Galileya dzina lace N azarete,

27. kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, dzina lace Yosefe, wa pfuko la Davine; ndipo dzina lace la namwaliyo ndilo Mariya.

Werengani mutu wathunthu Luka 1