Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. POPEZA ambiri anayesa kulongosola nkhani ya zinthu zinacitika pakati pa ife,

2. monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,

3. kuyambira paciyambi, ndinayesa nkokoma inenso, amene ndinalondalonda mosamalitsa zinthu zonse kuyambira paciyambi, kulembera kwa iwe tsatane tsatane, Teofilo wabwinotu iwe;

4. kuti udziwitse zoona zace za mau amene unaphunzira.

5. Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lace Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wace wa ana akazi a pfuko la Aroni, dzina lace Elisabeti.

6. Ndipo onse awiri anali olungama mtima pamaso pa Mulungu, namayendabe m'malamulo onse ndi zoikika za Ambuye osacimwa.

Werengani mutu wathunthu Luka 1