Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. POPEZA ambiri anayesa kulongosola nkhani ya zinthu zinacitika pakati pa ife,

2. monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,

3. kuyambira paciyambi, ndinayesa nkokoma inenso, amene ndinalondalonda mosamalitsa zinthu zonse kuyambira paciyambi, kulembera kwa iwe tsatane tsatane, Teofilo wabwinotu iwe;

4. kuti udziwitse zoona zace za mau amene unaphunzira.

5. Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lace Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wace wa ana akazi a pfuko la Aroni, dzina lace Elisabeti.

6. Ndipo onse awiri anali olungama mtima pamaso pa Mulungu, namayendabe m'malamulo onse ndi zoikika za Ambuye osacimwa.

7. Ndipo analibe mwana, popeza Elisabeti anali wouma, ndipo onse awiri anakalamba.

8. Ndipo panali, pakucita iye nchito yakupereka nsembe m'dongosolo la gulu lace, pamaso pa Mulungu, monga mwa macitidwe a kupereka nsembe,

9. adamgwera maere akufukiza zonunkhira polowa iye m'Kacisi wa Ambuye.

10. Ndipo khamu lonse la anthu Iinalikupemphera kunja nthawi ya zonunkhira.

Werengani mutu wathunthu Luka 1