Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Filemoni 1:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Inde, mbale, ndikondwere nawe mwa Ambuye: utsitsimutse mtima wanga mwa Kristu.

21. Pokhulupirira kumvera kwako ndikulembera iwe, podziwa kuti udzacicanso koposa cimene ndinena.

22. Koma undikonzerenso pogona; pakuti ndiyembekeza kuti mwa mapemphero anu ndidzapatsidwa kwa inu.

23. Epafra wandende mnzanga mwa Kristu Yesu akulankhula iwe;

24. ateronso, Marko, Aristarko, Dema, Luka, anchito anzanga.

Werengani mutu wathunthu Filemoni 1