18. Koma ngati anakulakwira kanthu, kapena wakongola kanthu, undiwerengere ine kameneko;
19. Ine Paulo ndicilemba ndi dzanja langa, ndidzacibwezera ine; kuti ndisanene nawe kuti iwe ndiwe mangawa anga.
20. Inde, mbale, ndikondwere nawe mwa Ambuye: utsitsimutse mtima wanga mwa Kristu.
21. Pokhulupirira kumvera kwako ndikulembera iwe, podziwa kuti udzacicanso koposa cimene ndinena.
22. Koma undikonzerenso pogona; pakuti ndiyembekeza kuti mwa mapemphero anu ndidzapatsidwa kwa inu.
23. Epafra wandende mnzanga mwa Kristu Yesu akulankhula iwe;
24. ateronso, Marko, Aristarko, Dema, Luka, anchito anzanga.
25. Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale pamodzi ndi mzimu wanu. Amen.