Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Filemoni 1:17-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ngati tsono undiyesa woyanjana nawe, umlandire iye monga ine mwini.

18. Koma ngati anakulakwira kanthu, kapena wakongola kanthu, undiwerengere ine kameneko;

19. Ine Paulo ndicilemba ndi dzanja langa, ndidzacibwezera ine; kuti ndisanene nawe kuti iwe ndiwe mangawa anga.

20. Inde, mbale, ndikondwere nawe mwa Ambuye: utsitsimutse mtima wanga mwa Kristu.

21. Pokhulupirira kumvera kwako ndikulembera iwe, podziwa kuti udzacicanso koposa cimene ndinena.

22. Koma undikonzerenso pogona; pakuti ndiyembekeza kuti mwa mapemphero anu ndidzapatsidwa kwa inu.

23. Epafra wandende mnzanga mwa Kristu Yesu akulankhula iwe;

24. ateronso, Marko, Aristarko, Dema, Luka, anchito anzanga.

25. Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale pamodzi ndi mzimu wanu. Amen.

Werengani mutu wathunthu Filemoni 1