1. PAULO, wandende wa Kristu Yesu, ndi Timoteo mbaleyo, kwa Filemoni wokondedwayo ndi wanchito mnzathu,
2. ndi kwa Apiya mlongoyo, ndi Arkipo msilikari mnzathu, ndi kwa Mpingo uli m'nyumba yako;
3. Cisomo kwa inu ndi mtendere za kwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Kristu.
4. Ndiyamika Mulungu wanga nthawi zonse, ndi kukumbukila iwe m'mapemphero anga,