Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 6:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ndinaona pamene Mwanawankhosa anamasula cimodzi ca zizindikilo zisanu ndi ziwiri, ndipo ndinamva cimodzi mwa zamoyo zinai, nicinena, ngati mau a bingu, Idza.

2. Ndipo ndinapenya, ndipo taonani, kavalo woyera, ndipo womkwerayo anali nao uta; ndipo anampatsa korona; ndipo anaturukira wolakika kuti alakike.

3. Ndipo pamene anamasula cizindikilo caciwiri, ndinamva camoyo caciwiri nicinena, Idza.

4. Ndipo anaturuka kavalo wina, wofiira: ndipo anampatsa iye womkwera mphamvu yakucotsa mtendere pa dziko ndi kuti aphane; ndipo anampatsa iye lupanga lalikuru.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 6