1. Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Sarde lemba:Izi anena iye wakukhala nayo mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu, ndi nyenyezi zisanu ndi riwiri: Ndidziwa nchito zako, kuti uli nalo dzina lakuti uli ndi moyo, ndipo uli wakufa.
2. Khala wodikira, ndipo limbitsa zotsalira, zimene zinafuna kufa; pakutisindinapeza nchito zako zakufikira pamaso pa Mulungu wanga.
3. Cifukwa cace kumbukila umo unalandira nunamvamo; nusunge nulape. Ukapanda kudikira tsono, ndidzafika ngati mbala, ndipo sudzazindikira nthawi yace ndidzadza pa iwe.
4. Komatu uli nao maina owerengeka m'Sarde, amene sanadetsa zobvala zao; ndipo adzayenda ndi Ine m'zoyera; cifukwa ali oyenera.
5. Iye amene alakika adzambveka motero zobvala zoyera; ndipo sindidzafafaniza ndithu dzina lace m'buku la moyo, ndipo ndidzambvomereza dzina lace pamaso pa Atate wanga, ndi pamaso pa angelo ace.