Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 21:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo 1 pamzinda sipafunika dzuwa, kapena mwezi wakuuwalira; pakuti ulemerero wa Mulungu uunikira umenewu, ndipo nyali yace ndiye Mwanawankhosa.

24. Ndipo 2 amitundu adzayendayenda mwa kuunika kwace; ndi mafumu a dziko atenga ulemerero wao kulowa nao momwemo.

25. Ndipo 3 pa zipata zace sipatsekedwa konse usana, 4 (pakuti sikudzakhala usiku komweko);

26. ndipo 5 adzatenga ulemerero ndi ulemu wa amitundu nadzalowa nao momwemo;

27. ndipo 6 simudzalowa konse momwemo kanthu kali konse kosapatulidwa kapena iye wakucita conyansa ndi bodza; koma iwo okha olembedwa 7 m'buku la moyo la Mwanawankhosa.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 21