Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 2:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo ndidzaononga ana ace ndi imfa; ndipo idzazindikira Mipingo yonse kuti 3 ine ndine iye amene ayesa imso ndi mitima; ndipo 4 ndidzaninkha kwa yense wa inu monga mwa nchito zanu.

24. Koma ndinena kwa inu, kwa otsala a ku Tiyatira, onse amene alibe ciphunzitso ici, amene sanazindikira zakuya za Satana, monga anena, Sindikusanjikizani katundu wina.

25. Koma 5 cimene muli naco, gwirani kufikira ndikadza.

26. Ndipo iye amene alakika, ndi iye amene asunga nchito zanga kufikira citsiriziro, kwa iye 6 ndidzapatsa ulamuliro wa pa amitundu;

27. ndipo 7 adzawalamulira ndi ndodo yacitsulo, monga zotengera za woumba mbiya ziphwanyika mapale; monga lnenso ndalandira kwa Atate wanga;

28. ndipo ndidzampatsa iye 8 nthanda.

29. Iye wokhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 2