Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 2:20-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Komatu ndiri nako kotsutsana ndi iwe, cuti ulola mkazi 2 Yezebeli, wodzieha zekha mneneri; ndipo aphunzitsa, nasokeretsa akapolo anga, kuti acite cigololo ndi kudya zoperekedwa nsenbe kwa mafano.

21. Ndipo ndanpatsa iye nthawi kuti alape; koma safuna kulapa kusiyana naco cigololo cace.

22. Taona, ndimponya iye pakama, ndi iwo akucita cigololo naye kuwalonga m'cisautso cacikuru, ngati salapa iwo ndi kuleka nchito zace.

23. Ndipo ndidzaononga ana ace ndi imfa; ndipo idzazindikira Mipingo yonse kuti 3 ine ndine iye amene ayesa imso ndi mitima; ndipo 4 ndidzaninkha kwa yense wa inu monga mwa nchito zanu.

24. Koma ndinena kwa inu, kwa otsala a ku Tiyatira, onse amene alibe ciphunzitso ici, amene sanazindikira zakuya za Satana, monga anena, Sindikusanjikizani katundu wina.

25. Koma 5 cimene muli naco, gwirani kufikira ndikadza.

26. Ndipo iye amene alakika, ndi iye amene asunga nchito zanga kufikira citsiriziro, kwa iye 6 ndidzapatsa ulamuliro wa pa amitundu;

27. ndipo 7 adzawalamulira ndi ndodo yacitsulo, monga zotengera za woumba mbiya ziphwanyika mapale; monga lnenso ndalandira kwa Atate wanga;

28. ndipo ndidzampatsa iye 8 nthanda.

29. Iye wokhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 2