Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 17:16-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo nyanga khumi udaziona, ndi cirombo, izi zidzadana ndi mkazi wacigololoyo, nizidzamkhalitsa wabwinja wausiwa, nizidzadya nyama yace, nizidzampsereza ndi moto.

17. Pakuti Mulungu anapatsa kumtima kwao kucita za m'mtima mwace, ndi kucita ca mtima umodzi ndi kupatsa ufumu wao kwa cirombo, kufikira akwaniridwa mau a Mulungu.

18. Ndipo mkaziyo unamuona, ndiye mudzi waukuru, wakucita ufumu pa mafumu a dziko.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 17