Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 11:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipoanandipatsa ine bango ngati ndodo, ndikuti, Tanyamuka, nuyese Kacisi wa Mulungu, ndi guwa la nsembe, ndi iwo akulambiramo.

2. Ndipo bwalo la kunja kwa Kacisi ulisiye padera, osaliyesa; pakuti adapatsa ilo kwa amitundu; ndipo mzinda wopatulika adzaupondereza miyezi makumi anai mphambu iwiri.

3. Ndipo ndidzalamulira mboni zanga ziwiri, ndipo zidzanenera masiku cikwi cimodzi ndi mazana awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi, zobvala ciguduli.

4. Izo ndizo mitengo iwiri ya azitona ndi zoikapo nyali ziwiri zakuima pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 11