Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 10:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ndinaona mngelo wina wolimba alikutsika Kumwamba, wobvala mtambo; ndi utawaleza pamutu pace, ndi nkhope yace ngati dzuwa, ndi mapazi ace ngati mizati yamoto;

2. ndipo anali nako m'dzanja lace kabuku kofunyulula: ndipo anaponda nalo phazi lace lamanja panyanja,

3. ndi Iamanzerelo pamtunda, napfuula ndi mau akuru, monga ngati mkango ubangula; ndipo pamene anapfuula mabingu asanu ndi awiri analankhula mau ao.

4. Ndipo pamene adalankhula mabingu asanu ndi awiriwo, ndinati ndilembe; ndipo udinamva mau ocokera Kumwamba nanena, Sindikiza naco cizindikilo zimene adalankhula mabingu asanu ndi limodzi, ndipo usazilembe,

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 10