Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 10:1-2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ndinaona mngelo wina wolimba alikutsika Kumwamba, wobvala mtambo; ndi utawaleza pamutu pace, ndi nkhope yace ngati dzuwa, ndi mapazi ace ngati mizati yamoto;

2. ndipo anali nako m'dzanja lace kabuku kofunyulula: ndipo anaponda nalo phazi lace lamanja panyanja,

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 10