Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 1:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Taonani, adza ndi mitambo; ndipo diso liri lonse lidzampenya iye, iwonso amene anampyoza; ndipo mafuko onse a pa dziko adzamlira iye. Terotu. Amen.

8. Ine ndine Alefa ndi Omega, ati Ambuye Mulungu, amene ali, amene adali, ndi amene alinkudza, Wamphamvuyonse.

9. Ine Yohane, mbale wanu ndi woyanjana nanu m'cisautso ndi ufumu ndi cipiriro zokhala m'Yesu, ndinakhala pa cisumbu cochedwa Patmo, cifukwa ca mao a Mulungu ndi umboni wa Yesu.

10. Ndinagwidwa ndi Mzimu tsiku la Ambuye, ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mau akuru, ngati a lipenga,

11. ndi kuti, Cimene upenya, lemba m'buku, nulitumize kwa Mipingo isanu ndi iwiri, ku Efeso, ndi ku Smurna, ndi ku Pergamo, ndi ku Tiyatira, ndi ku Sarde, ndi ku Filadelfeya, ndi ku Laodikaya.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 1