Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 1:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Yohane kwa Mipingo isanu ndi wiri m'Asiya: Cisomo kwa inu ndi ntendere, zocokerakwa iye amene ili, ndi amene adali, ndi amene aliikudza; ndi kwa mizimu isanu ndi wiri yokhala ku mpando wacifumu vace;

5. ndi kwa Yesu Kristu, mboli yokhulupirikayo, wobadwa woyanba wa akufa, ndi mkulu wa mafunu a dziko lapansi, Kwa iye ameieatikonda ife, natimasula ku macimo athu ndi mwazi wace;

6. natiyesa ife ufumu tikhale ansembe a Mulungu ndiye Atate wace; kwa iye kukhale ulemerero ndi mphamvu kufikira nthawi za nthawi. Amen.

7. Taonani, adza ndi mitambo; ndipo diso liri lonse lidzampenya iye, iwonso amene anampyoza; ndipo mafuko onse a pa dziko adzamlira iye. Terotu. Amen.

8. Ine ndine Alefa ndi Omega, ati Ambuye Mulungu, amene ali, amene adali, ndi amene alinkudza, Wamphamvuyonse.

9. Ine Yohane, mbale wanu ndi woyanjana nanu m'cisautso ndi ufumu ndi cipiriro zokhala m'Yesu, ndinakhala pa cisumbu cochedwa Patmo, cifukwa ca mao a Mulungu ndi umboni wa Yesu.

10. Ndinagwidwa ndi Mzimu tsiku la Ambuye, ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mau akuru, ngati a lipenga,

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 1