Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 9:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. kapena cifukwa ali mbeu ya Abrahamu, siali onse ana; koma anati, Mwa Isake, mbeu yako idzaitanidwa.

8. Ndiko kuti, ana a thupi sakhala iwo ana a Mulungu ai; koma ana a lonjezo awerengedwa mbeu yace.

9. Pakuti mau a lonjezo ndi amenewa, Pa nyengo iyi ndidzadza, ndipo Sara adzakhala ndi mwana

10. Ndipo si cotero cokha, koma Rebekanso, pamene anali ndi pakati pa mmodzi, ndiye kholo lathu Isake;

11. pakuti anawo asanabadwe, kapena asanacite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, si cifukwa ca nchito ai, koma cifukwa ca wakuitanayo,

12. cotero kunanenedwa kwa uyo, Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.

13. Inde monga kunalembedwa, Ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.

Werengani mutu wathunthu Aroma 9