Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 9:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti ndikadafunakuti ine ndekha nditembereredwe kundicotsa kwa Kristu cifukwa ca abale anga, ndiwo a mtundu wanga monga mwa thupi;

4. ndiwo Aisrayeli; ali nao umwana, ndi ulemerero, ndi mapangano, ndi kupatsa kwa malamulo, ndi kutumikira m'kacisi wa Mulungu, ndi malonjezo;

5. a iwo ali makolo, ndi kwa iwo anacokera Kristu, monga mwa thupi, ndiye Mulungu wa pamwamba pa zonse wolemekezeka ku nthawi zonse. Amen.

6. Koma sikuli ngati mau a Mulungu anakhala cabe ai. Pakuti onse akucokera kwa a Israyeli siali Israyeli;

7. kapena cifukwa ali mbeu ya Abrahamu, siali onse ana; koma anati, Mwa Isake, mbeu yako idzaitanidwa.

8. Ndiko kuti, ana a thupi sakhala iwo ana a Mulungu ai; koma ana a lonjezo awerengedwa mbeu yace.

Werengani mutu wathunthu Aroma 9