Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 9:20-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma munthu iwe, ndiwe yani wakubwezera Mulungu mau? Kodi cinthu copangidwa cidzanena ndi amene anacipanga, U ndipangiranji ine cotero?

21. Kodi kapena woumba mbiya sakutha kucita zace padothi, kuumba ndi ncinci yomweyo cotengera cimodzi caulemu ndi cina camanyazi?

22. Ndipo titani ngati Mulungu, pofuna iye kuonetsa mkwiyo wace, ndi kudziwitsa mph amvu yace, analekerera ndi cilekerero cambiri zotengera za mkwiyo zokonzekera cionongeko?

23. ndi kuti iye akadziwitse ulemerero wace waukuru pa zotengera zacifundo, zimene iye anazikonzeratu kuulemerero,

24. ndi ife amenenso iye anatiitana, si a mwa Ayuda okha okha, komanso a mwa anthu amitundu?

25. Monga atinso mwa Hoseya,Amene sanakhala anthu anga, ndidzawacha anthu anga;Ndi iye amene sanali wokondedwa, wokondedwa.

26. 1 Ndipo kudzali, kuti pamalo pamenepo kunanenedwa kwa iwo, Simuli anthu anga ai,Pomwepo iwo adzachedwa ana a Mulungu wamoyo.

27. Ndipo Yesaya apfuula za Israyeli, kuti,2 Ungakhale unyinji wa ana a Israyeli ukhala monga mcenga wa kunyanja, 3 cotsalira ndico cidzapulumuka.

28. Pakuti Ambuye adzacita mau ace pa dziko lapansi, kuwatsiriza mwacidule.

29. Ndipo monga Yesaya anati kale,4 Ngati Ambuye wa makamu a kumwamba sanatisiyira ife mbeu,Tikadakhala monga Sodoma, ndipo tikadafanana ndi Gomora.

30. Cifukwa cace tidzatani? 5 Kuti amitundu amene sanatsata cilungamo, anafikira cilungamo, ndico cilungamo ca cikhulupiriro;

31. 6 koma Israyeli, potsata lamulo la cilungamo, sanafikira lamulolo.

32. Cifukwa canji? Cifukwa kuti sanacitsata ndi cikhulupiriro, koma monga ngati ndi nchito. 7 Anakhumudwa pa mwala wokhumudwitsa;

33. monganso kwalembedwa, kuti,8 Onani, ndikhazika m'Ziyoni mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;Ndipo 9 wakukhulupirira iye sadzacita manyazi.

Werengani mutu wathunthu Aroma 9