Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 9:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pamenepo udzanena ndine kodi, Adandaulabe bwanji? Pakuti ndani anakaniza cifuno cace?

20. Koma munthu iwe, ndiwe yani wakubwezera Mulungu mau? Kodi cinthu copangidwa cidzanena ndi amene anacipanga, U ndipangiranji ine cotero?

21. Kodi kapena woumba mbiya sakutha kucita zace padothi, kuumba ndi ncinci yomweyo cotengera cimodzi caulemu ndi cina camanyazi?

22. Ndipo titani ngati Mulungu, pofuna iye kuonetsa mkwiyo wace, ndi kudziwitsa mph amvu yace, analekerera ndi cilekerero cambiri zotengera za mkwiyo zokonzekera cionongeko?

23. ndi kuti iye akadziwitse ulemerero wace waukuru pa zotengera zacifundo, zimene iye anazikonzeratu kuulemerero,

24. ndi ife amenenso iye anatiitana, si a mwa Ayuda okha okha, komanso a mwa anthu amitundu?

25. Monga atinso mwa Hoseya,Amene sanakhala anthu anga, ndidzawacha anthu anga;Ndi iye amene sanali wokondedwa, wokondedwa.

26. 1 Ndipo kudzali, kuti pamalo pamenepo kunanenedwa kwa iwo, Simuli anthu anga ai,Pomwepo iwo adzachedwa ana a Mulungu wamoyo.

27. Ndipo Yesaya apfuula za Israyeli, kuti,2 Ungakhale unyinji wa ana a Israyeli ukhala monga mcenga wa kunyanja, 3 cotsalira ndico cidzapulumuka.

Werengani mutu wathunthu Aroma 9