Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 9:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. pakuti anawo asanabadwe, kapena asanacite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, si cifukwa ca nchito ai, koma cifukwa ca wakuitanayo,

12. cotero kunanenedwa kwa uyo, Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.

13. Inde monga kunalembedwa, Ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.

14. Ndipo tsono tidzatani? Kodi ciripo cosalungama ndi Mulungu? Msatero ai.

15. Pakuti anati ndi Mose, Ndidzacitira cifundo amene ndimcitira cifundo, ndipo ndidzakhala ndi cisoni kwa iye amene ndikhala naye cisoni.

Werengani mutu wathunthu Aroma 9