Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 7:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. koma ucimo, pamene unapeza cifukwa, unacita m'kati mwanga zilakolako zonse mwa lamulo; pakuti popanda lamulo ucimo uli wakufa.

9. Ndipo kale ine ndinali wamoyo popanda lamulo; koma pamene lamulo linadza, ucimo unatsitsimuka, ndipo ine ndinafa.

10. Ndipo lamulo, limene linali Iakupatsa moyo, ndinalipeza lakupassa imfa.

11. Pakuti ucimo, pamene unapeza cifukwa mwa lamulo, unandinyenga ine, ndi kundipha nalo.

12. Cotero cilamulo ciri coyera, ndi cilangizo cace ncoyera, ndi colunaama, ndi cabwino.

13. Ndipo tsopano cabwino cija cinandikhalira imfa kodi? Msatero ai. Koma ucimo, kuti uoneke kuti uli ucimo, wandicitira imfa mwa cabwino cija; kuti ucimo ukakhale wocimwitsa ndithu mwa lamulo.

14. Pakuti tidziwa kuti cilamulo ciri cauzimu; koma ine ndiri wathupi, wogulitsidwa kapolo wa ucimo.

15. Pakuti cimene ndicita sindicidziwa; pakuti sindicita cimene ndifuna, koma cimene ndidana naco, ndicita ici.

16. Koma ngati ndicita cimene sindicifuna, ndibvomerezana naco cilamulo kuti ciri cabwino.

17. Ndipo tsopano si ine ndicicita, koma ucimo wakukhalabe m'kati mwanga ndiwo.

18. Pakuti ndidziwa kuti m'kati mwanga, ndiko m'thupi langa, simukhala cinthu cabwino; pakuti kufuna ndiri nako, koma kucita cabwino sindikupeza.

19. Pakuti cabwino cimene ndicifuna, sindicicita; koma coipa cimene sindicifuna, cimeneco ndicicita.

Werengani mutu wathunthu Aroma 7