Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 5:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo si cotero cokha, koma ife tikondwera ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Kristu, amene talandira naye tsopano ciyanjanitso.

12. Cifukwa cace, monga ucimo unalowa m'dziko lapansi mwa munthu mmodzi, ndi imfa mwa ucimo; cotero imfa inafikira anthu onse, cifukwa kuti onse anacimwa.

13. Pakuti kufikira nthawi ya lamulo ucimo unali m'dziko lapansi; koma ucimo suwerengedwa popanda lamulo.

14. Komatu imfa inacita ufumu kuyambira kwa Adamu kufikira kwa Mose, ngakhale pa iwonso amene sanacimwa monga macimwidwe ace a Adamu, ndiye fanizo la wakudzayo.

Werengani mutu wathunthu Aroma 5