13. M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;
14. M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;
15. Miyendo yao icita liwiro kukhetsa mwazi;
16. Kusakaza ndi kusauka kuli m'njira zao;
17. Ndipo njira ya mtendere sanaidziwa;
18. Kumuopa Mulungu kulibe pamaso pao.
19. Ndipo tidziwa kuti zinthu ziri zonse cizinena cilamulo cizilankhulira iwo ali naco cilamulo; kuti pakamwa ponse patsekedwe, ndi dziko lonse lapansi litsutsidwe ndi Mulungu;
20. cifukwa kuti pamaso pace palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi Debito za lamulo; pakuti ucimo udziwika ndi lamulo.