Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 3:11-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;

12. Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.

13. M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;

14. M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;

15. Miyendo yao icita liwiro kukhetsa mwazi;

16. Kusakaza ndi kusauka kuli m'njira zao;

17. Ndipo njira ya mtendere sanaidziwa;

18. Kumuopa Mulungu kulibe pamaso pao.

19. Ndipo tidziwa kuti zinthu ziri zonse cizinena cilamulo cizilankhulira iwo ali naco cilamulo; kuti pakamwa ponse patsekedwe, ndi dziko lonse lapansi litsutsidwe ndi Mulungu;

20. cifukwa kuti pamaso pace palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi Debito za lamulo; pakuti ucimo udziwika ndi lamulo.

21. Koma tsopano cilungamo ca Mulungu caoneka copanda lamulo, cilamulo ndi aneneri acitira ici umboni;

22. ndico cilungamo ca Mulungu cimene cicokera mwa cikhulupiriro ca pa Yesu Kristu kwa onse amene akhulupira; pakuti palibe kusiyana;

23. pakuti onse anacimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu;

24. ndipo ayesedwa olungama kwaulere, ndi cisomo cace, mwa ciombolo ca mwa Kristu Yesu;

25. amene Mulungu anamuika poyera akhale cotetezera mwa cikhulupiriro ca m'mwazi wace, kuti aonetse cilungamo cace, popeza Mulungu m'kulekerera kwace analekerera macimo ocitidwa kale lomwe;

26. kuti aonetse cilungamo cace m'nyengo yatsopano; kuti iye akhale wolungama, ndi wakumuyesa wolungama iye amene akhulupirira Yesu,

Werengani mutu wathunthu Aroma 3