Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 2:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma kolingana ndi kuuma kwako, ndi mtima wako wosalapa, ulikudziunjikira wekha mkwiyo pa dzuwa la mkwiyo ndi la kubvumbulutsa kuweruza kolungama kwa Mulungu;

6. amene adzabwezera munthu ali yense kolingana ndi nchito zace;

7. kwa iwo amene afunafuna ulemerero ndi ulemu ndi cisaonongeko, mwa kupirira pa nchito zabwino, adzabwezera moyo wosatha;

8. koma kwa iwo andeu, ndi osamvera coonadi, koma amvera cosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

9. nsautso ndi kuwawa mtima, kwa moyo wa munthu ali yense wakucita zoipa, kuyambira Myuda, komanso Mhelene;

10. koma ulemerero ndi ulemu ndi mtendere kwa munthu ali yense wakucita zabwino, kuyambira Myuda, ndiponso Mhelene;

11. pakuti Mulungu alibe tsankhu.

12. Pakuti onse amene anacimwa opanda lamulo adzaonongeka opanda lamulo; ndi onse amene anacimwa podziwa lamulo adzaweruzidwa ndi lamulo;

Werengani mutu wathunthu Aroma 2