Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 2:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Pakuti dzina la Mulungu licitidwa mwano cifukwa ca inu, pakati pa anthu a mitundu, monga mwalembedwa.

25. Pakuti inde mdulidwe uli wabwino, ngati iwe umacita lamulo; koma ngati uli wolakwira lamulo, mdulidwe wako wasanduka kusadulidwa.

26. Cifukwa cace ngati wosadulidwa asunga zoikika za cilamulo, kodi kusadulidwa kwace sikudzayesedwa ngati mdulidwe?

27. Ndipo kusadulidwa, kumene kuli kwa cibadwidwe, ngati kukwanira cilamulo, kodi sikudzatsutsa iwe, amene uli nao malembo ndi mdulidwe womwe, ndiwe wolakwira lamulo?

28. Pakuti siali Myuda amene akhala wotere pamaso, kapena suli mdulidwe umene uli wotere pamaso, m'thupimo;

29. koma Myuda ndiye amene akhala wotere mumtima; ndipo mdulidwe uli wa mtima, mumzimu, si m'malembo ai; kuyamika kwace sikucokera kwa anthu, koma kwa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Aroma 2