Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 2:23-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Iwe wakudzitamandira pacilamulo, kodi ucitira Mulungu mwano ndi kulakwa kwako m'cilamulo?

24. Pakuti dzina la Mulungu licitidwa mwano cifukwa ca inu, pakati pa anthu a mitundu, monga mwalembedwa.

25. Pakuti inde mdulidwe uli wabwino, ngati iwe umacita lamulo; koma ngati uli wolakwira lamulo, mdulidwe wako wasanduka kusadulidwa.

26. Cifukwa cace ngati wosadulidwa asunga zoikika za cilamulo, kodi kusadulidwa kwace sikudzayesedwa ngati mdulidwe?

27. Ndipo kusadulidwa, kumene kuli kwa cibadwidwe, ngati kukwanira cilamulo, kodi sikudzatsutsa iwe, amene uli nao malembo ndi mdulidwe womwe, ndiwe wolakwira lamulo?

Werengani mutu wathunthu Aroma 2