Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 2:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa cace uli wopanda mau owiringula, munthu iwe, amene uli yense wakuweruza; pakuti m'mene uweruza wina, momwemo udzitsutsa iwe wekha, pakuti iwe wakuweruza, umacita zomwezo.

2. Ndipo tidziwa kuti kuweruza kwa Mulungu kuli koona pa iwo akucita zotere.

3. Ndipo uganiza kodi, munthu iwe, amene umaweruza iwo akucita zotere, ndipo uzicitanso iwe mwini, kuti udzapulumuka pa mlandu wit Mulungu?

4. Kapena upeputsa kodi kulemera kwa ubwino wace, ndi cilekerero ndi cipiriro cace, wosadziwa kuti ubwino wa Mulungu ukubwezera kuti ulape?

5. Koma kolingana ndi kuuma kwako, ndi mtima wako wosalapa, ulikudziunjikira wekha mkwiyo pa dzuwa la mkwiyo ndi la kubvumbulutsa kuweruza kolungama kwa Mulungu;

6. amene adzabwezera munthu ali yense kolingana ndi nchito zace;

7. kwa iwo amene afunafuna ulemerero ndi ulemu ndi cisaonongeko, mwa kupirira pa nchito zabwino, adzabwezera moyo wosatha;

8. koma kwa iwo andeu, ndi osamvera coonadi, koma amvera cosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

9. nsautso ndi kuwawa mtima, kwa moyo wa munthu ali yense wakucita zoipa, kuyambira Myuda, komanso Mhelene;

10. koma ulemerero ndi ulemu ndi mtendere kwa munthu ali yense wakucita zabwino, kuyambira Myuda, ndiponso Mhelene;

11. pakuti Mulungu alibe tsankhu.

Werengani mutu wathunthu Aroma 2