Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 15:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Cifukwa cace mulandirane wina ndi mnzace, monganso Kristu anakulandirani inu, kukacitira Mulungu ulemerero.

8. Ndipo ndinena kuti Kristu anakhala mtumiki wa mdulidwe, cifukwa ca coonadi ca Mulungu, kuti alimbikitse malonjezo opatsidwa kwa makolo,

9. ndi kuti anthu a mitundu yina akalemekeze Mulungu, cifukwa ca cifundo; monga kwalembedwa,Cifukwa ca icindidzakubvomerezani Inu pakati pa anthu amitundu,Ndidzayimbira dzina lanu.

10. Ndiponso anena,Kondwani, amitundu inu, pamodzindi anthu ace.

11. Ndiponso,Tamandani Ambuye, inu a mitundu yonse;Ndipo anthu onse amtamande.

12. Ndiponso, Yesaya ati,Padzali muzu wa Jese,Ndi iye amene aukira kucita ufumu pa anthu amitundu;Iyeyo anthu amitundu adzamuyembekezera.

13. Ndipo Mulungu wa ciyembekezo adzaze inu ndi cimwemwe conse ndi mtendere m'kukhulupira, kuti mukacuruke ndi ciyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

14. Koma ine ndekhanso, abale anga, nditsimikiza mtima za inu, kuti inu nokhanso muli odzala ndi ubwino, odzazidwa ndi kudziwitsa konse, ndi kukhoza kudandaulirana wina ndi mnzace.

Werengani mutu wathunthu Aroma 15