Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 15:22-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Cifukwa cacenso ndinaletsedwa kawiri kawiri kudza kwa inu;

23. koma tsopano, pamene ndiribe malo m'maiko akuno, ndipo pokhala ndi kulakalaka zaka zambiri kudza kwa inu, ndidzatero,

24. pamene pali ponse ndidzapita ku Spanya. Pakuti ndiyembekeza kuonana ndi inu pa ulendo wanga, ndi kuperekezedwa ndi inu panjira panga kumeneko, ngati nditayamba kukhuta pang'ono ndi kukhala ndi inu.

25. Koma 1 tsopano ndipita ku Yerusalemu, ndirikutumikira oyera mtima.

26. Pakuti 2 kunakondweretsa a ku Makedoniya ndi Akaya kucereza osauka a kwa oyera mtima a ku Yerusalemu.

27. Pakuti kunakondweretsa iwo; ndiponso iwo ali amangawa ao. 3 Pakuti ngati amitundu anagawana zinthu zao zauzimu, alinso amangawa akutumikica iwo ndi zinthu zathupi.

28. Koma pamene ndikatsiriza ici, ndi kuwasindikizira iwo cipatso ici, ndidzapyola kwanu kupita ku Spanya.

29. Ndipo 4 ndidziwa kuti pamene ndikadza kwanu, ndidzafika m'kudzaza kwace kwa cidalitso ca Kristu.

Werengani mutu wathunthu Aroma 15