Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 15:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma mwina ndaposa kukulemberani molimba mtima monga kukukumbutsaninso, cifukwa ca cisomo capatsidwa kwa ine ndi Mulungu,

16. kuti ndikhale mtumiki wa Yesu Kristu kwa anthu amitundu, wakutumikira Uthenga Wabwino wa Mulungu, kuti kupereka kwace kwa anthu amitundu kulandirike, koyeretsedwa ndi Mzimu Woyera.

17. Cifukwa cace ndiri naco codzitamandira ca m'Kristu Yesu ndi zinthu za kwa Mulungu.

18. Pakuti sindingathe kulimba mtima kulankhula zinthu zimene Kristu sanazicita mwa ine zakumveretsa anthu amitundu, ndi mau ndi nchito,

Werengani mutu wathunthu Aroma 15