Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 14:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pakuti tingakhale tiri ndi moyo, tikhalira Ambuye moyo; kapena tikafa, tifera Ambuye; cifukwa cace tingakhale tiri ndi moyo, kapena tikafa, tikhala ace a Ambuye.

9. Pakuti, cifukwa ca ici Kristu adafera, nakhalanso ndi moyo, kuti iye akakhale Ambuye wa akufa ndi wa amoyo.

10. Koma iwe uweruziranji mbale wako? kapena iwenso upeputsiranji mbale wako? pakuti ife tonse tidzaimirira ku mpando wakuweruza wa Mulungu.

11. Pakuti kwalembedwa,Pali moyo wanga, ari Ambuye, mabondo onse adzagwadira Ine,Ndipo malilime onse adzabvomereza Mulungu,

12. Cotero munthu ali yense wa ife adzadziwerengera mlandu wace kwa Mulungu.

13. Cifukwa cace risaweruzanenso wina mnzace; koma weruzani ici makamaka, kuti munthu asaike cokhumudwitsa pa njira ya mbale wace, kapena compunthwitsa.

14. Ndidziwa, ndipo ndakhazikika mtima mwa Ambuye Yesu, kuti palibe cinthu conyansa pa cokha; koma kwa ameneyo aciyesa conyansa, kwa iye cikhala conyansa.

Werengani mutu wathunthu Aroma 14