Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 11:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. monga kunalembedwa kuti, Mulungu anawapatsa mzimu watulo, maso kuti asapenye, ndi makutu kuti asamve, kufikira lero lino.

9. Ndipo Davide akuti,Gome lao likhale kwa iwo, ngati msampha, ndi ngati diwa,Ndi monga cokhumudwitsa, ndi cowabwezera cilango;

10. Maso ao adetsedwe, kuti asapenye,Ndipo muweramitse msana wao masiku onse.

11. Cifukwa cace ndinena, Anakhumudwa kodi kuti agwe? Msatero ai; koma ndi kulakwa kwao cipulumutso cinadza kwa anthu akunja, kudzacititsa iwo nsanje.

12. Ndipo ngati kulakwa kwao kwatengera dzikolapansi zolemera, ndipo kucepa kwao klltengera anthu amitundu zolemera; koposa kotani nanga kudzaza kwao?

13. Koma ndilankhula ndi inu anthu amitundu. Popeza ine ndiri mtumwi wa anthu amitundu, millemekeza utumiki wanga;

14. kuti ngati nkutheka ndikacititse nsanje amenewo a mtundu wanga; ndi kupulumutsa ena a iwo.

15. Pakuti ngati kuwataya kwao kuli kuvanianitsa kwa dziko lapansi, nanga kulandiridwa kwao kudzatani, koma ndithu ngati moyo wakucokera kwa: akufa?

16. Ndipo ngati zoundukula ziri zopatulika, coteronso mtanda; ndipo ngati muzu uli wopatulika, coteronso nthambi.

17. Koma ngati nthambi zina zinathyoledwa, ndipo iwe, ndiwe mtengo wazitona wa kuthengo, unamezetsanidwa mwa izo, nugawana nazo za muzu za mafuta ace a mtengowo,

18. usadzitama iwe wekha pa nthambizo: koma ngati udzitama wekha, suli iwe amene unyamula muzu, ai, koma muzu ukunyamula iwetu.

19. Ndipo kapena udzanena, Nthambizo zathyoledwa kuti ine ndikamezetsanidwe nao.

Werengani mutu wathunthu Aroma 11