Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 10:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti Mose walemba kuti munthu amene acita cilungamo ca m'lamulo, adzakhala naco ndi moyo.

6. Koma cilungamo ca cikhulupiriro citero, Usamanena mumtima mwako, Adzakwera ndani Kumwambako? ndiko, kutsitsako Kristu;

7. kapena, Adzatsikira ndani kudzenieko? ndiko, kukweza Kristu kwa akufa.

8. Koma citani? Mau ali pafupi ndiwe, m'kamwa mwako, ndi mumtima mwako; ndiwo mau a cikhulupiriro, amene ife tiwalalikira:

9. kuti ngati udzabvomereza m'kamwa mwako Yesu ndiye Ambuye, ndi kukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka:

10. pakuti ndi mtima munthu akhulupira kutengapo cilungamo; ndi m'kamwa abvomereza kutengapo cipulumutso

11. Pakuti lembo litere, Amene ali yense akhulupirira iye, sadzacita manyazi.

12. Pakuti kulibe kusiyana Myuda ndi Mhelene; pakuti Yemweyo ali Ambuye wa onse, nawacitira zolemera onse amene aitana pa iye;

Werengani mutu wathunthu Aroma 10