Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 10:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti lembo litere, Amene ali yense akhulupirira iye, sadzacita manyazi.

12. Pakuti kulibe kusiyana Myuda ndi Mhelene; pakuti Yemweyo ali Ambuye wa onse, nawacitira zolemera onse amene aitana pa iye;

13. pakuti, amene ali yense adzaitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.

14. Ndipo iwo adzaitana bwanji pa iye amene sanamkhulupirira? ndipo adzakhulupirira bwanji iye amene sanamva za iye? ndipo adzamva bwanji wopanda wolalikira?

15. ndipo adzalalikira bwanji, ngati satumidwa? monganso kwalembedwa, Okometsetsa ndithu ali mapazi a iwo akulalikira Uthenga Wabwino wa zinthu zabwino.

Werengani mutu wathunthu Aroma 10