Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 10:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Abale, kufunitsa kwa mtima wanga ndi pemphero langa limene ndiwapempherera kwa Mulungu, ndilo, kuti apulumuke.

2. Pakuti ndiwacitira iwo umboni kuti a ali ndi cangu ca kwa Mulungu, koma si monga mwa cidziwitso.

3. Pakuti pakusadziwa cilungamo ca Mulungu, ndipo pofuna kukhazikitsa cilungamo ca iwo okha, iwo sanagonja ku cilungamo ca Mulungu.

4. Pakuti Kristu ali cimariziroca lamulo kulinga kucilungamo kwa amene ali yense akhulupira,

5. Pakuti Mose walemba kuti munthu amene acita cilungamo ca m'lamulo, adzakhala naco ndi moyo.

6. Koma cilungamo ca cikhulupiriro citero, Usamanena mumtima mwako, Adzakwera ndani Kumwambako? ndiko, kutsitsako Kristu;

7. kapena, Adzatsikira ndani kudzenieko? ndiko, kukweza Kristu kwa akufa.

Werengani mutu wathunthu Aroma 10