9. Pakuti Mulungu ali mboni yanga, amene ndimtumikira mu mzimu wanga, m'Uthenga Wabwino wa Mwana wace, kuti kosalekeza ndikumbukila inu, ndi kupempha masiku onse m'mapemphero anga,
10. ngati nkutheka tsopano mwa cifuniro ca Mulungu, ndione ulendo wabwino, wakudza kwa inu.
11. Pakuti ndilakalaka kuonana ndinu, kuti ndikagawire kwa inu mtulo wina wauzimu, kuti inu mukhazikike;
12. ndiko, kuti ine ndikatonthozedwe pamodzi ndi inu, mwa cikhulupiriro ca ife tonse awiri, canu ndi canga.