Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Akolose 4:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ambuye inu, citirani akapolo anu colungama ndi colingana; podziwa kuti inunso muli naye Mbuye m'Mwamba.

2. Citani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi ciyamiko;

3. ndi kutipempherera ifenso pomwepo, kuti Mulungu atitsegulire ife pakhomo pa mau, kuti tilankhule cinsinsi ca Kristu; cimenenso ndikhalira m'ndende,

4. kuti ndicionetse ici monga ndiyenera kulankhula.

5. Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kucita macawi nthawi ingatayike.

6. Mau anu akhale m'cisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akarani.

7. Zonse za kwa ine adzakuzindikiritsani Tukiko, mbale wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika ndi kapolo mnzanga mwa Ambuye:

Werengani mutu wathunthu Akolose 4