Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 7:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo kuli ngati kunena, mwa Abrahamu Levinso wakulandira limodzi limodzi la magawo khumi adapereka limodzi la magawo khumi;

10. pakuti pajapo anali m'cuuno ca atate wace, pamene Melikizedeke anakomana naye.

11. Ndipo pakadakhala ungwiro mwa unsembe wa Cilevi (pakuti momwemo anthu analandira cilamulo), pakadatsala kusowa kotani kuti auke wansembe wina monga mwa dongosolo la Melikizedeke, wosayesedwa monga mwa dongosolo la Aroni?

12. Pakuti posandulika unsembe, kufunikanso kuti lamulo lisandulike.

13. Pakuti iye amene izi zineneka za iye, akhala wa pfuko lina, wa ili palibe munthu watumikira guwa la nsembe.

14. Pakuti kwadziwikadi kuti Ambuye wathu anaturuka mwa Yuda; za pfuko ili Mose sanalankhula kanthu ka ansembe.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 7