Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 7:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. koma iye amene mawerengedwe a cibadwidwe cace sacokera mwa iwo, anatenga limodzi la magawo khumi kwa Abrahamu, namdalitsa iye amene ali nao malonjezano.

7. Ndipo popanda citsutsano konse wamng'ono adalitsidwa ndi wamkuru.

8. Ndipo pano anthu ofeka alandira limodzi la magawo khumi; koma apo iye, woti adamcitira umboni kuti ali ndi moyo.

9. Ndipo kuli ngati kunena, mwa Abrahamu Levinso wakulandira limodzi limodzi la magawo khumi adapereka limodzi la magawo khumi;

10. pakuti pajapo anali m'cuuno ca atate wace, pamene Melikizedeke anakomana naye.

11. Ndipo pakadakhala ungwiro mwa unsembe wa Cilevi (pakuti momwemo anthu analandira cilamulo), pakadatsala kusowa kotani kuti auke wansembe wina monga mwa dongosolo la Melikizedeke, wosayesedwa monga mwa dongosolo la Aroni?

Werengani mutu wathunthu Ahebri 7