Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti mkulu wa ansembe ali yense, wotengedwa mwa anthu, amaikika cifukwa ca anthu m'zinthu za kwa Mulungu, kuti apereke mitulo, ndiponso nsembe, cifukwa ca macimo:

2. akhale wokhoza kumva cifundo ndi osadziwa ndi olakwa, popeza iye yekhanso amazingwa ndi cifoko;

3. ndipo cifukwa caceco ayenera, monga m'malo a anthuwo, moteronso m'malo a iye yekha, kupereka nsembe cifukwa ca macimo.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 5